Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

21 Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu,
    chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!
Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake
    ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake.
            Sela
Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka
    ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.
Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa
    masiku ochuluka kwamuyaya.
Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu;
    Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.
Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya,
    Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.
Pakuti mfumu imadalira Yehova;
    kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba,
    iyo sidzagwedezeka.

Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse;
    dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.
Pa nthawi ya kuonekera kwanu
    mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha.
Mu ukali wake Yehova adzawameza,
    ndipo moto wake udzawatha.
10 Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi,
    zidzukulu zawo pakati pa anthu.
11 Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo
    sadzapambana;
12 pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo
    pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.

13 Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu,
    ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.