Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

14 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
    “Kulibe Mulungu.”
Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;
    palibe amene amachita zabwino.

Yehova kumwamba wayangʼana pansi,
    kuyangʼana anthu onse
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
    amene amafunafuna Mulungu.
Onse atembenukira kumbali,
    onse pamodzi asanduka oyipa;
palibe amene amachita zabwino,
    palibiretu ndi mmodzi yemwe.

Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?
    Akudya anthu anga ngati chakudya chawo
    ndipo satamanda Yehova?
Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,
    pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,
    koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.

Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!
    Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,
    Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!