Add parallel Print Page Options

112 Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,
    amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
    mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
    ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
    wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
    amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

Ndithu sadzagwedezeka;
    munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
    mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
    potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
    chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
    nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
    adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
    Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.