Add parallel Print Page Options

Pemphero la Habakuku

Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;
    Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.
Muzichitenso masiku athu ano,
    masiku athu ano zidziwike;
    mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,
    Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.
            Sela
Ulemerero wake unaphimba mlengalenga
    ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;
    kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,
    mʼmene anabisamo mphamvu zake.
Patsogolo pake pankagwa mliri;
    nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;
    anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.
Mapiri okhazikika anagumuka
    ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.
    Njira zake ndi zachikhalire.
Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,
    mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?
    Kodi munakalipira timitsinje?
Kodi munapsera mtima nyanja
    pamene munakwera pa akavalo anu
    ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Munasolola uta wanu mʼchimake,
    munayitanitsa mivi yambiri.
            Sela
Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
10     mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.
Madzi amphamvu anasefukira;
    nyanja yozama inakokoma
    ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,
    pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,
    pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,
    ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu,
    kukapulumutsa wodzozedwa wanu.
Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,
    munawononga anthu ake onse.
            Sela
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake
    pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,
ankasangalala ngati kuti akudzawononga
    osauka amene akubisala.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,
    kuvundula madzi amphamvu.

16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,
    milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;
mafupa anga anaguluka,
    ndipo mawondo anga anawombana.
Komabe ndikuyembekezera mofatsa,
    tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,
    ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.
Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,
    ndipo mʼminda musatuluke kanthu.
Ngakhale nkhosa
    ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,
    ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;
    amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,
    amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.